4 Lilime la mwana woyamwa limamatira kumalakalaka kwace ndi ludzu;Ana ang'ono apempha mkate koma palibe wakuwanyemera.
5 Omwe anadya zolongosoka angosiyidwa m'makwalala;Omwe analeredwa nabvekedwa mlangali afungatira madzala.
6 Pakuti mphulupulu ya mwana wamkazi wa anthu amtundu wanga, ikula koposa cimo la Sodomu,Umene unapasuka m'kamphindi, anthu osaucitira kanthu.
7 Omveka ace anakonzeka koposa cipale cofewa, nayera koposa mkaka,Matupi ao anafiira koposa timiyala toti pyu; maonekedwe ao ananga a safiro wa mtengo wapatari.
8 Maonekedwe ao ada koposa makala, sazindikirika m'makwalala;Khungu lao limamatira pa mafupa ao, lakhwinyata, lasanduka ngati ndodo.
9 Ophedwa ndi lupanga amva bwino kupambana ophedwa ndi njala;Pakuti amenewa angokwalika napyozedwa, posowa zipatso za m'munda.
10 Manja a akazi acisoni anaphika anaanao;Anali cakudya cao poonongeka mwana wamkazi wa anthu a mtundu wanga.