Maliro 1 BL92

Tsoka la Yerusalemu

1 Ha! mudziwo unadzala anthu, ukhalatu pa wokha!Ukunga mkazi wamasiye!Waukuruwo mwa amitundu, kalonga wamkazi m'madera a dzikoWasanduka wolamba!

2 Uliralira usiku; misozi yace iri pa masaya ace;Mwa onse amene anaukonda mulibe mmodzi wakuutonthoza:Mabwenzi ace onse aucitira ziwembu,Asanduka adani ace.

3 Yuda watengedwa ndende cifukwa ca msauko ndi ukapolo waukuru;Akhala mwa amitundu, sapeza popuma;Onse akumlondola anampeza pakati popsinjikiza.

4 M'njira za Ziyoni mulira posoweka akudzera msonkhano;Pa zipata zace zonse papasuka; ansembe ace onse ausa moyo;Anamwali ace asautsidwa; iye mwini namva zowawa.

5 Amaliwongo ace asanduka akuru ace, adani ace napindula;Pakuti Yehova wamsautsa pocuruka zolakwa zace;Ana ace ang'ono alowa m'ndende pamaso pa adani ace.

6 Ulemu wace wonse wamcokera mwana wamkazi wa Ziyoni;Akalonga ace asanduka nswala zosapeza busa,Anayenda opanda mphamvu pamaso pa wompitikitsa.

7 M'masiku a msauko wace ndi kusocera kwaceYerusalemu ukumbukira zokondweretsa zace zonse zacikhalire;Pogwidwa anthu ace ndi mdaniyo popanda wakuupulumutsa,Adaniwo anamuona naseka mwacipongwe mabwinja ace.

8 Yerusalemu wacimwa kwambiri; cifukwa cace wasanduka cinthu conyansa;Onse akuulemekeza aupeputsa, pakuti auona wamarisece;Inde, uusa moyo, nubwerera m'mbuyo.

9 Udio wace unali m'nsaru zace; sunakumbukira citsiriziro cace;Cifukwa cace watsika mozizwitsa; ulibe wakuutonthoza;Taonani Yehova, msauko wanga, pakuti mdaniyo wadzikuzayekha.

10 Amaliwongo atambasulira manja ao pa zokondweretsa zace zonse;Pakuti waona amitundu atalowa m'malo ace opatulika,Amene munalamulira kuti asalowe mumsonkhano mwanu.

11 Anthu ace onse ausa moyo nafunafuna mkate;Ndi zokondweretsa zao agula zakudya kuti atsitsimutse moyo wao;Taonani, Yehova, nimupenye; pakuti ndasanduka wonyansa.

12 Kodi muyesa cimeneci cabe, nonsenu opita panjira?Penyani nimuone, kodi ciripo cisoni cina ngati cangaci amandimvetsa ine,Cimene Yehova wandisautsa naco tsiku la mkwiyo wace waukali?

13 Anatumiza moto wocokera kumwamba kulowa m'mafupa anga, unawagonjetsa;Wachera mapazi anga ukonde, wandibwezera m'mbuyo;Wandipululutsa ndi kundilefula tsiku lonse.

14 Gori la zolakwa zanga lamangidwa ndi dzanja lace;Zalukidwa, zakwera pakhosi panga; iye wakhumudwitsa mphamvuyanga;Ambuye wandipereka m'manja mwao, sindithai kuwalaka.

15 Ambuye wapepula ngwazi zanga zonse pakati panga;Waitanira msonkhano pa ine kuti uphwanye anyamata anga,Ambuye wapondereza namwaliyo, mwana wamkazi wa Ziyoni, monga mopondera mphesa.

16 Cifukwa ca zimenezi ndilira; diso langa, diso langatu likudza madzi:Pakuti wonditonthoza, wotsitsimutsa moyo wanga, anditarikira;Ana anga asungulumwa, pakuti adaniwo apambana.

17 Ziyoni atambasula manja ace, palibe wakumtonthoza;Yehova walamulira kuti omzungulira Yakobo akhale adani ace;Yerusalemu wasanduka cinthu conyansa pakati pao.

18 Yehova ali wolungama; pakuti ndapikisana ndi m'kamwa mwace:Mudtvetu, mitundu ya anthu nonsenu, nimuone cisoni canga;Anamwali ndi anyamata anga atha kulowa m'ndende.

19 Ndinaitanaakundikondawokoma anandinyenga;Ansembe ndi akulu anga anamwalira m'mudzimu,Alikufunafuna zakudya zotsitsimutsa miyoyo yao.

20 Onani, Yehova; pakuti ndabvutika, m'kati mwanga mugwedezeka;Mtima wanga wasanduka mwa ine; pakuti ndapikisana nanu ndithu;Kunjako lupanga limangopha ana; m'nyumba muli imfa.

21 Iwo anamva kuti ndiusa moyo, palibe wonditonthoza;Adani anga onse atha kumva msauko wanga, nakondwera kuti mwatero ndinu;Mudzafikitsa tsiku lija mwalichula, ndipo iwowo adzanga ine.

22 Zoipa zao zonse zidze pamaso panu,Muwacitire monga mwandicitira ine cifukwa ca zolakwa zanga zonse,Pakuti ndiusa moyo kwambiri, ndi kulefuka mtima wanga,

Mitu

1 2 3 4 5