5 Maere ako awiri akunga ana awiri a nswala obadwa limodzi,Akudya pakati pa akakombo.
6 Mpaka dzuwa litapepa, mithunzi ndi kutanimpha,Ndikamuka ku phiri la nipa,Ndi ku citunda ca mtanthanyerere.
7 Wakongola monse monse, wokondedwa wanga, namwaliwe,Mulibe cirema mwa iwe.
8 Idza nane kucokera ku Lebano, mkwatibwi,Kucokera nane ku Lebano:Unguza pamwamba pa Amana,Pa nsonga ya Seniri ndi Hermoni,Pa ngaka za mikango,Pa mapiri a anyalugwe.
9 Walanda mtima wanga, mlongwanga, mkwatibwi;Walanda mtima wanga ndi diso lako limodzi,Ndi cinganga cimodzi ca pakhosi pako,
10 Ha, cikondi cako ncokongola, mlongwanga, mkwatibwi!Kodi cikondi cako siciposa vinyo?Kununkhira kwa mphoka yako ndi kuposa zonunkhiritsa za mitundu mitundu!
11 M'milomo yako, mkwatibwi, mukukha uci,Uci ndi mkaka ziri pansi pa lilime lako;Kununkhira kwa zobvala zako ndi kunga kununkhira kwa Lebano,