Nyimbo 2 BL92

1 Ndine duwa lofiira la ku Saroni,Ngakhale kakombo wa kuzigwa.

2 Ngati kakombo pakati pa mingaMomwemo wokondedwa wanga pakati pa ana akazi.

3 Ngati maula pakati pa mitengo ya m'nkhalango,Momwemo wokondedwa wanga pakati pa ana amuna.Ndinakondwa pakukhala pa mthunzi wace,Zipatso zace zinatsekemera m'kamwa mwanga.

4 Anandifikitsa ku nyumba ya vinyo,Mbendera yace yondizolimira inali cikondi.

5 Mundilimbikitse ndi mphesa zouma, munditonthoze mtima ndi maula,Pakuti ndadwala ndi cikondi.

6 Dzanja lace lamanzere anditsamiritse kumutu,Dzanja lace lamanja ndi kundifungatira.

7 Ndikulumbirirani, ana akazi inu a ku Yerusalemu,Pali mphoyo, ndi nswala za kuthengo,Kuti musautse, ngakhale kugalamutsa cikondi,Mpaka cikafuna mwini.

8 Mau a wokondedwa wanga mnyamatayo! Taona, adza,Alikulumpha pamapiri, alikujidimuka pazitunda.

9 Wokondedwa wanga akunga mphoyo, pena mwana wa mbawala:Taona, aima patseri pa khoma pathu,Apenyera pazenera, Nasuzumira pamade.

10 Wokondedwa wanga analankhula, nati kwa ine,Tauka, bwenzi langa, wokongola wanga, tiye.

11 Pakuti, taona, cisanu catha,Mvula yapita yaleka;

12 Maluwa aoneka pansi;Nthawi yoyimba mbalame yafika,Mau a njiwa namveka m'dziko lathu;

13 Mkuyu uchetsa nkhuyu zace zosakhwima,Mipesa niphuka,Inunkhira bwino.Tauka, bwenzi langa, wokongola wangawe, tiyetu.

14 Nkhunda yangawe, yokhala m'ming'alu ya thanthwe, mobisika motsetsereka,Ndipenye nkhope yako, ndimve manako;Pakuti mau ako ngokoma, nkhope yako ndi kukongola.

15 Mutigwirire ankhandwe, ngakhale ang'ono, amene akuononga minda yamipesa;Pakuti m'minda yathu yamipesa muphuka biriwiri.

16 Wokondedwa wanga ndi wa ine, ine ndine wace:Aweta zace pakati pa akakombo,

17 Mpaka dzuwa litapepa, mithunzi ndi kutanimpha,Bwera, bwenzi langawe, nukhale ngati mphoyo pena mwana wa mbawalaPa mapiri a mipata.

Mitu

1 2 3 4 5 6 7 8