7 Madzi ambiri sangazimitse cikondi,Ngakhale mitsinje yodzala kucikokolola:Mwamuna akapereka katundu yense wa m'nyumba yace ngati sintho la cikondi,Akanyozedwa ndithu.
8 Tiri ndi mlongwathu wamng'ono,Alibe maere;Ticitirenji mlongwathuTsiku lokhoma unkhoswe wace?
9 Ngati ndiye khoma, tidzamanga pa iye nsanja yasiliva:Ngati ndiye citseko tidzamtsekereza ndi matabwa amikungudza.
10 Ndine khoma, maere anga akunga nsanja zace:Pamaso pa mnyamatayo ndinafanana ngati wopeza mtendere.
11 Solomo anali ndi munda wamipesa ku Baalahamoni;Nabwereka alimi mundawo;Yense ambwezere ndalama cikwi cifukwa ca zipatso zace.
12 Koma munda wanga wamipesa, uli pamaso panga ndiwo wangatu;Naco cikwico, Solomo iwe,Koma olima zipatso zace azilandira mazana awiri.
13 Namwaliwe wokhala m'minda,Anzake amvera mau ako:Nanenso undimvetse.