11 Kwa iye kukhale mphamvu ku nthawi za nthawi. Amen.
12 Mwa Silvano, mbale wathu wokhulupirika monga ndimayesa, ndalembera kwa inu mwacidule, ndi kudandaulira, ndi kucita umboni, kuti cisomo coona ca Mulungu ndi ici; m'cimeneci muimemo.
13 Iye wa ku Babulo wosankhidwa pamodzi nanu akulankhulani; ateronso Marko mwana wanga.
14 Lankhulanani ndi cipsompsono ca cikondi.Mtendere ukhale ndi inu nonse muli mwa Kristu.