4 woweruza bwino nyumba yace ya iye yekha, wakukhala nao ana ace omvera iye ndi kulemekezeka konse.
5 Koma ngati munthu sadziwa kuweruza nyumba ya iye yekha, adzasunga bwanji Mpingo wa Mulungu?
6 Asakhale wophunza, kuti podzitukumula ungamgwere mlandu wa mdierekezi.
7 Kuyeneranso kuti iwo akunja adzakhoza kumcitira umboni wabwino; kuti ungamgwere mtonzo, ndi msampha wa mdierekezi.
8 Momwemonso atumiki akhale olemekezeka, osanena pawiri, osamwetsa vinyo, osati a cisiriro conyansa;
9 okhala naco cinsinsi ca cikhulupiriro m'cikumbu mtima coona.
10 Koma iwonso ayambe ayesedwe; pamenepo atumikire, akakhala opanda cifukwa.