5 Koma ngati munthu sadziwa kuweruza nyumba ya iye yekha, adzasunga bwanji Mpingo wa Mulungu?
6 Asakhale wophunza, kuti podzitukumula ungamgwere mlandu wa mdierekezi.
7 Kuyeneranso kuti iwo akunja adzakhoza kumcitira umboni wabwino; kuti ungamgwere mtonzo, ndi msampha wa mdierekezi.
8 Momwemonso atumiki akhale olemekezeka, osanena pawiri, osamwetsa vinyo, osati a cisiriro conyansa;
9 okhala naco cinsinsi ca cikhulupiriro m'cikumbu mtima coona.
10 Koma iwonso ayambe ayesedwe; pamenepo atumikire, akakhala opanda cifukwa.
11 Momwemonso akazi akhale olemekezeka, osadierekeza, odzisunga, okhulupirika m'zonse.