10 Pakuti kukalingako tlgwiritsa nchito ndi kuyesetsa, cifukwa ciyembekezo cathu tiri naco pa Mulungu wamoyo, amene ali Mpulumutsi wa anthu onse, makamaka wa okhulupira.
11 Lamulira izi, nuziphunzitse.
12 Munthu asapeputse ubwana wako; komatu khala citsanzo kwa iwo okhulupira, m'mau, m'mayendedwe, m'cikondi, m'cikhulupiriro, m'kuyera mtima.
13 Kufikira ndidza ine, usamalire kuwerenga, kucenjeza, kulangiza.
14 Usanyalapse mphatsoyo iri mwa iwe, yopatsidwa kwa iwe mwa cinenero, pamodzi ndi kuika kwa manja a akulu.
15 Izi uzisamalitse; mu izi ukhale; kuti kukula mtima kwako kuonekere kwa onse.
16 Udzipenyerere wekha, ndi ciphunzitsoco. Uzikhala muizi; pakuti pocita ici udzadzipulumutsa iwe wekha ndi iwo akumva iwe.