5 Pakuti ici mucidziwe kuti wadama yense, kapena wacidetso, kapena wosirira, amene apembedza mafano, alibe colowa m'ufumu wa Kristu ndi Mulungu.
6 Asakunyengeni inu munthu ndi mau opanda pace, pakuti cifukwa ca hi umadza mkwiyo wa Mulungu pa ana a kusamvera.
7 Cifukwa cace musakhale olandirana nao;
8 pakuti kale munali mdima, koma tsopano muli kuunika mwa Ambuye; yendani monga ana a kuunika,
9 pakuti cipatso ca kuunika ticipeza m'ubwino wonse, ndi cilungamo, ndi coonadi,
10 kuyesera cokondweretsa Ambuye nciani;
11 ndipo musayanjane nazo nchito za mdima zosabala kanthu, koma maka-makanso muzitsutse;