8 pakuti kale munali mdima, koma tsopano muli kuunika mwa Ambuye; yendani monga ana a kuunika,
9 pakuti cipatso ca kuunika ticipeza m'ubwino wonse, ndi cilungamo, ndi coonadi,
10 kuyesera cokondweretsa Ambuye nciani;
11 ndipo musayanjane nazo nchito za mdima zosabala kanthu, koma maka-makanso muzitsutse;
12 pakuti zocitidwa nao m'tseri, kungakhale kuzinena kucititsa manyazi.
13 Koma zinthu zonse potsutsika ndi kuunika, zionekera; pakuti conse cakuonetsa ciri kuunika.
14 Mwa ici anena, Khala maso wogona iwe, nuuke kwa akufa, ndi, po Kristu adzawala pa iwe.