1 Ananu, mverani akukubalani mwa Ambuye, pakuti ici ncabwino.
2 Lemekeza atate wako ndi amako (ndilo lamulo loyamba lokhala nalo lonjezano),
3 kuti kukhale bwino ndi iwe, ndi kuti ukhale wa nthawi yaikuru padziko.
4 Ndipo atate inu, musakwiyitse ana anu; komatu muwalere iwo m'maleredwe ndi cilangizo ca Ambuye.