1 Ananu, mverani akukubalani mwa Ambuye, pakuti ici ncabwino.
2 Lemekeza atate wako ndi amako (ndilo lamulo loyamba lokhala nalo lonjezano),
3 kuti kukhale bwino ndi iwe, ndi kuti ukhale wa nthawi yaikuru padziko.
4 Ndipo atate inu, musakwiyitse ana anu; komatu muwalere iwo m'maleredwe ndi cilangizo ca Ambuye.
5 Akapolo inu, mverani iwo amene ali ambuye anu monga mwa thupi, ndi kuwaopa ndi kunthunthumira nao, ndi mtima wanu wosakumbukila kanthu kena, monga kwa Kristu;
6 si monga mwa ukapolo wa pamaso, monga okondweretsa anthu, komatu monga akapolo a Kristu, akucita cifuniro ca Mulungu cocokera kumtima;
7 akucita ukapolo ndi kubvomereza mtima, monga kutumikira Yesu Kristu, si anthu ai;