20 Ana a Gibara, makumi asanu ndi anai mphambu asanu.
21 Ana a Betelehemu zana limodzi mphambu makumi awiri kudza atatu.
22 Anthu a ku Netofa, makumi asanu mphambu asanu ndi mmodzi.
23 Anthu a ku Anatoti, zana limodzi mphambu makumi awiri kudza asanu ndi atatu.
24 Ana a Azimaveti, makumi anai mphambu awiri.
25 Ana a Kiriyati Arimu, Kefira, ndi Beeroti, mazana asanu ndi awiri mphambu makumi anai kudza atatu.
26 Ana a Rama ndi Gaba, mazana asanu ndi limodzi mphambu makumi awiri kudza mmodzi.