4 Ana a Sefatiya, mazana atatu mphambu makumi asanu ndi awiri kudza awiri.
5 Ana a Ara, mazana asanu ndi awiri mphambu makumi asanu ndi awiri kudza asanu.
6 Ana a Pahati Moabu, a ana a Yesuwa ndi Yoabu, zikwi ziwiri mphambu mazana asanu ndi atatu kudza khumi ndi awiri.
7 Ana a Elamu, cikwi cimodzi mphambu mazana awiri kudza makumi asanu ndi anai.
8 Ana a Zatu, mazana asanu ndi anai mphambu makumi anai kudza asanu.
9 Ana a Zakai, mazana asanu ndi awiri mphambu makumi asanu ndi limodzi.
10 Ana a Bani, mazana asanu ndi limodzi mphambu makumi anai kudza awiri.