4 inde, analimbana ndi wamthenga nampambana; analira, nampembedza Iye; anampeza Iye ku Beteli, ndi kumeneko Iye analankhula ndi ife;
5 ndiye Yehova Mulungu wa makamu, cikumbukilo cace ndi Yehova.
6 M'mwemo utembenukire kwa Mulungu wako, sunga cifundo ndi ciweruzo, nuyembekezere Mulungu wako kosalekeza.
7 Ndiye Mkanani, m'dzanja lace muli miyeso yonyenga, akonda kusautsa.
8 Ndipo Efraimu anati, Zedi ndasanduka wolemera, ndadzionera cuma m'nchito zonse ndinazigwira; sadzapeza mwa ine mphulupulu yokhala cimo.
9 Koma Ine ndine Yehova Mulungu wako cicokere dziko la Aigupto, ndidzakukhalitsanso m'mahema, monga masiku a masonkhano oikika.
10 Ndalankhulanso ndi aneneri, ndipo Ine ndacurukitsa masomphenya; ndi pa dzanja la aneneri ndinanena ndi mafanizo.