4 Koma munthu asatsutsane ndi mnzace, kapena kudzudzula mnzace; popeza anthu ako ndiwo akunga otsutsana ndi wansembe.
5 Ndipo udzakhumudwa usana, ndi mneneri yemwe adzakhumudwa pamodzi ndi iwe usiku; ndipo ndidzaononga mai wako.
6 Anthu anga aonongeka cifukwa ca kusadziwa; popeza unakana kudziwa, Inenso ndikukaniza, kuti usakhale wansembe wanga; popeza waiwala cilamulo ca Mulungu wako, Inenso ndidzaiwala ana ako.
7 Monga anacuruka, momwemo anandicimwira; ndidzasanduliza ulemerero wao ukhale manyazi.
8 Adyerera cimo la anthu anga, nakhumbira cosalungama cao, yense ndi mtima wace.
9 Ndipo kudzakhala monga anthu, momwemo wansembe; ndipo ndidzawalanga cifukwa canjira zao, ndi kuwabwezera macitidwe ao.
10 Ndipo adzadya, koma osakhuta; adzacita cigololo, koma osacuruka; pakuti waleka kusamalira Yehova.