9 Momwemonso, akazi adzibveke okha ndi cobvala coyenera, ndi manyazi, ndi cidziletso; osati ndi tsitsi lace loluka, ndi golidi kapena ngale, kapena maraya a mtengo wace wapatali;
10 komatu (umo mokomera akazi akubvomereza kulemekeza Mulungu), mwa nchito zabwino.
11 Mkazi aphunzire akhale wacete m'kumvera konse.
12 Koma sindilola ine kuti mkazi aphunzitse, kapena kulamulira mwamuna; komatu akhale cete.
13 Pakuti Adamu anayamba kulengedwa, pamenepo Heva;
14 ndipo Adamu sananyengedwa, koma mkaziyo ponyengedwa analowa m'kulakwa;
15 koma adzapulumutsidwa mwa kubala mwana, ngati akhala m'cikhulupiriro ndi cikondi ndi ciyeretso pamodzi ndi cidziletso.