4 Pakuti colengedwa conse ca Mulungu ncabwino, ndipo palibe kanthu kayenera kutayika, ngati kalandiridwa ndi ciyamiko;
5 pakuti kayeretsedwa ndi Mau a Mulungu ndi kupemphera.
6 Ngati ukumbutsa abale zinthu izi, udzakhala mtumiki wabwino wa Kristu Yesu, woleredwa m'mauwo a cikhulupiriro, ndi malangizo abwino amene udawatsata;
7 koma nkhani zacabe ndi za akazi okalamba ukane. Ndipo udzizoloweretse kucita cipembedzo;
8 pakuti cizolowezi ca thupi cipindula pang'ono, koma cipembedzo cipindula zonse, popeza cikhala nalo Lonjezano la ku moyo uno, ndi la moyo ulinkudza.
9 Okhulupirika mauwa ndi oyenera kulandiridwa konse.
10 Pakuti kukalingako tlgwiritsa nchito ndi kuyesetsa, cifukwa ciyembekezo cathu tiri naco pa Mulungu wamoyo, amene ali Mpulumutsi wa anthu onse, makamaka wa okhulupira.