5 pakuti kayeretsedwa ndi Mau a Mulungu ndi kupemphera.
6 Ngati ukumbutsa abale zinthu izi, udzakhala mtumiki wabwino wa Kristu Yesu, woleredwa m'mauwo a cikhulupiriro, ndi malangizo abwino amene udawatsata;
7 koma nkhani zacabe ndi za akazi okalamba ukane. Ndipo udzizoloweretse kucita cipembedzo;
8 pakuti cizolowezi ca thupi cipindula pang'ono, koma cipembedzo cipindula zonse, popeza cikhala nalo Lonjezano la ku moyo uno, ndi la moyo ulinkudza.
9 Okhulupirika mauwa ndi oyenera kulandiridwa konse.
10 Pakuti kukalingako tlgwiritsa nchito ndi kuyesetsa, cifukwa ciyembekezo cathu tiri naco pa Mulungu wamoyo, amene ali Mpulumutsi wa anthu onse, makamaka wa okhulupira.
11 Lamulira izi, nuziphunzitse.