3 ndipo ndidzalikha woweruza pakati pace, ndi kupha akalonga ace onse, ati Yehova.
4 Atero Yehova, Cifukwa ca zolakwa zitatu za Yuda, kapena zinai, sindidzabweza kulanga kwace; popeza akaniza cilamulo ca Yehova, osasunga malemba ace; ndipo awalakwitsa mabodza ao amene makolo ao anawatsata;
5 koma ndidzatumiza moto pa Yuda, udzanyeketsa nyumba zacifumu za m'Yerusalemu.
6 Atero Yehova, Cifukwa ca zolakwa zitatu za Israyeli, kapena zinai, sindidzabweza kulanga kwace; popeza agulitsa wolungama ndi ndalama, ndi wosowa cifukwa ca nsapato;
7 ndiwo amene aliralira pfumbi lapansi liri pamutu pa wosauka, napotoza njira ya wofatsa; ndipo munthu ndi atate wace amuka kwa namwali yemweyo, kuti aipse dzina langa loyera;
8 nagona pansi pa zopfunda za cikole ku maguwa a nsembe ali onse, ndi m'nyumba ya Mulungu wao akumwa vinyo wa iwo olipitsidwa.
9 Koma ndinaononga Ine pamaso pa Aamori, amene msinkhu wao unanga msinkhu wa mikungudza, nakhala nayo mphamvu ngati thundu; koma ndinaononga zipatso zao m'mwamba, ndi mizu yao pansi.