10 Pamenepo Amaziya wansembe wa ku Beteli anatumiza kwa Yerobiamu mfumu ya Israyeli, ndi kuti, Amosi wapangira inu ciwembu pakati pa nyumba ya Israyeli; dziko silikhoza kulola mau ace onse.
11 Pakuti atero Amosi, Yerobiamu adzafa ndi lupanga, ndi Israyeli adzatengedwadi ndende, kucoka m'dziko lace.
12 Amaziya anatinso kwa Amosi, Mlauli iwe, coka, thawira ku dziko la Yuda, nudye, nunenere komweko;
13 koma usaneneranso ku Beteli; pakuti pamenepo mpa malo opatulika a mfumu, ndiyo nyumba yacifumu.
14 Pamenepo Amosi anayankha, nati kwa Amaziya, Sindinali mneneri, kapena mwana wa mneneri, koma ndinali woweta ng'ombe, ndi wakuchera nkhuyu;
15 ndipo Yehova ananditenga ndirikutsata nkhosa, nati kwa ine Yehova, Muka, nenera kwa anthu anga Israyeli.
16 Cifukwa cace tsono, tamvera mau a Yehova, Iwe ukuti, Usamanenera cotsutsana ndi Israyeli, usadonthetsa mau akutsutsana ndi nyumba ya Isake;