3 Ndipo Yehova anacileka. Sicidzacitika, ati Yehova.
4 Ambuye Yehova anandionetsa cotere; ndipo taonani, Ambuye Yehova anaitana kuti atsutse ndi moto; ndipo unanyambita cakudya cacikuru ukadanyambitanso dziko.
5 Pamenepo ndinati, Ambuye Yehova, Iekanitu; Yakobo adzakhala ciriri bwanji? pakuti ali wamng'ono.
6 Ndipo Yehova anacileka. Ici comwe sicidiacitika, ati Ambuye Yehova.
7 Anandionetsa cotere; ndipo taonani, Ambuye anaima pa khoma lomangiwda ndi cingwe colungamitsira ciriri; ndi cingwe colungamitsira ciriri m'dzanja lace.
8 Ndipo Yehova anati kwa ine, Amosi, uona ciani? Ndipo ndinati, Cingwe colungamitsira ciriri. Nati Ambuye, Taona, ndidzaika cingwe colungamitsira ciriri pakati pa anthu anga Israyeli, sindidzawalekanso:
9 ndi misanje ya Isake idzakhala bwinja; ndi malo opatulika a Israyeli adzapasuka; ndipo ndidzaukira nyumba ya Yerobiamu ndi lupanga.