7 Anandionetsa cotere; ndipo taonani, Ambuye anaima pa khoma lomangiwda ndi cingwe colungamitsira ciriri; ndi cingwe colungamitsira ciriri m'dzanja lace.
8 Ndipo Yehova anati kwa ine, Amosi, uona ciani? Ndipo ndinati, Cingwe colungamitsira ciriri. Nati Ambuye, Taona, ndidzaika cingwe colungamitsira ciriri pakati pa anthu anga Israyeli, sindidzawalekanso:
9 ndi misanje ya Isake idzakhala bwinja; ndi malo opatulika a Israyeli adzapasuka; ndipo ndidzaukira nyumba ya Yerobiamu ndi lupanga.
10 Pamenepo Amaziya wansembe wa ku Beteli anatumiza kwa Yerobiamu mfumu ya Israyeli, ndi kuti, Amosi wapangira inu ciwembu pakati pa nyumba ya Israyeli; dziko silikhoza kulola mau ace onse.
11 Pakuti atero Amosi, Yerobiamu adzafa ndi lupanga, ndi Israyeli adzatengedwadi ndende, kucoka m'dziko lace.
12 Amaziya anatinso kwa Amosi, Mlauli iwe, coka, thawira ku dziko la Yuda, nudye, nunenere komweko;
13 koma usaneneranso ku Beteli; pakuti pamenepo mpa malo opatulika a mfumu, ndiyo nyumba yacifumu.