28 nandifikitsira cifundo pamaso pa mfumu, ndi aphungu ace, ndi pamaso pa akalonga amphamvu onse a mfumu. Motero ndinalimbika mtima, monga umo dzanja la Yehova Mulungu wanga linakhala pa ine; ndipo ndinasonkhanitsa mwa Israyeli anthu omveka akwere nane limodzi.