1 Ndipo akuru a nyumba za makolo ndi awa, ndi cibadwidwe ca iwo okwera nane limodzi kucokera ku Babulo, pokhala mfumu Aritasasta, ndi ici:
2 wa ana a Pinehasi, Gerisomu; wa ana a Itamara, Danieli; wa ana a Davide, Hatusi.
3 Wa ana a Sekaniya, wa ana a Parosi, Zekariya; ndi pamodzi naye, powawerenga monga mwa cibadwidwe cao, amuna zana limodzi mphambu makumi asanu.
4 Wa ana a Pahati Moabu, Elihoenai mwana wa Zerahiya; ndi pamodzi naye amuna mazana awiri.
5 Wa ana a Sekaniya, mwana wa Yahazieli; ndi pamodzi naye amuna mazana atatu.