1 MAU a Yehova amene anadza kwa Hoseya mwana wa Beeri masiku a Uziya, Yotamu, Ahazi, ndi Hezekiya, mafumu a Yuda, ndi masiku a Yerobiamu mwana wa Yoasi mfumu ya Israyeli.
2 Ciyambi ca kunena kwa Yehova mwa Hoseya, Ndipo Yehova anati kwa Hoseya, Muka, udzitengere mkazi wacigololo ndi ana acigololo; pakuti dziko latsata cigololo cokha cokha kuleka kutsata Yehova.
3 Ndipo anamuka natenga Gomeri mwana wamkazi wa Diblaimu; iye naima, nambalira mwana wamwamuna.
4 Ndipo Yehova anati kwa iye, Umuche dzina lace Yezreeli; pakuti katsala kanthawi, ndipo ndidzabwezera cilango mwazi wa Yezreeli pa nyumba ya Yehu, ndi kuleketsa ufumu wa nyumba ya Israyeli.
5 Ndipo kudzacitika tsiku lomwelo, ndidzatyola uta wa Israyeli m'cigwa ca Yezreeli.
6 Ndipo anaimanso, nabala mwana wamkazi. Ndipo Yehova anati kwa iye, Umuche dzina lace Wosacitidwacifundo; pakuti sindidzacitiranso cifundo nyumba ya Israyeli, kuti ndiwakhululukire konse.