6 Cifukwa cace taonani, ndidzacinga njira yako ndi minga, ndipo ndidzammangira mpanda, kuti asapeze mabande ace.
7 Ndipo adzatsata omkonda koma osawakumika, adzawafunafuna koma osawapeza; pamenepo adzati, Ndidzamuka ndi kubwererana ndi mwamuna wanga woyamba, popeza pamenepo panandikomera koposa tsopano.
8 Pakuti sanadziwa kuti ndine ndinampatsa tirigu, ndi vinyo, ndi mafuta, ndi kumcurukitsira siliva ndi golidi, zimene anapanga nazo Baala.
9 Cifukwa cace ndidzabwera ndi kucotsa tirigu wanga m'nyengo yace, ndi vinyo wanga m'nthawi yace yoikika, ndi kukwatula ubweya wanga ndi thonje langi, zimene zikadapfunda umarisece wace.
10 Ndipo tsopano ndidzaonetsa manyazi ace pamaso pa omkonda, popandanso wakumlanditsa m'dzanja langa.
11 Ndidzaleketsanso kusekerera kwace konse, madyerero ace, pokhala mwezi pace, ndi masabata ace, ndi masonkhano ace onse oikika.
12 Ndipo ndidzapasula mipesa yace ndi mikuyu yace, imene adanena, Iyi ndi mphotho yanga anandipatsa ondikondawo; ndipo ndidzaisandutsa thengo, ndi nyama zakuthengo zidzaidya.