3 Tidziwe tsono, tilondole kudziwa Yehova; kuturuka kwace kwakonzekeratu ngati matanda kuca; ndipo adzatidzera ngati mvula, ngati mvula ya masika yakuthirira dziko.
4 Efraimu iwe, ndidzakucitira ciani? Yuda iwe, ndikucitire ciani? pakuti kukoma mtima kwako kukunga mtambo wam'mawa ndi ngati mame akuphawa mamawa.
5 Cifukwa cace ndawalikha mwa aneneri; ndawapha ndi mau a pakamwa panga; ndi maweruzo anga aturuka ngati kuunika.
6 Pakuti ndikondwera naco cifundo, si nsembe ai; ndi kumdziwa Mulungu koposa nsembe zopsereza.
7 Koma iwo analakwira cipangano ngati Adamu, m'mene anandicitira monyenga.
8 Gileadi ndiwo mudzi wa ocita zoipa, wa mapazi a mwazi.
9 Ndipo monga magulu a mbala alalira munthu, momwemo msonkhano wa ansembe amapha pa njira ya ku Sekemu; indedi acita coipitsitsa.