1 Lipenga kukamwa kwako, Akudza ngati ciombankhanga, kulim bana ndi nyumba ya Yehova; cifukwa analakwira cipangano canga, napikisana naco cilamulo canga.
2 Adzapfuulira kwa Ine, Mulungu wanga, ife Aisrayeli tikudziwani.
3 Israyeli wacitaya cokoma, mdani adzamlondola.
4 Analonga mafumu, koma sikunacokera kwa Ine; anaika akalonga, koma sindinadziwa; anadzipangira mafano a siliva wao ndi golidi wao, kuti akalikhidwe.