1 Nchenche zakufa zinunkhitsa moipa nizioletsa mafuta onunkhira a sing'anga; comweco kupusa kwapang'ono kuipitsa iye amene achuka cifukwa ca nzeru ndi ulemu.
2 Wanzeru, mtima wace uli ku dzanja lace lamanja; koma citsiru, mtima wace kulamanzere.
3 Inde, poyendanso citsiru panjira, nzeru yace imthera ndipo angoti kwa onse kuti, Ndine citsiru.
4 Ngati mkuru akukwiyira, usasiye malo ako; cifukwa cifatso cipembedza utacimwa kwambiri.
5 Pali coipa ndaciona pansi pano, ngati kulakwa koyambira ndi mkuru;
6 utsiru ukhazikika pamwamba penipeni, ndipo olemera angokhala mwamanyazi.