Mlaliki 1 BL92

Za pansi pano nzacabe

1 MAU a Mlaliki, mwana wa Davide, mfumu ya m'Yerusalemu.

2 Zacabecabe, ati Mlaliki; zacabecabe zonse ndi cabe.

3 Kodi nchito zace zonse munthu asauka nazo zimpindulira ciani?

4 Mbadwo wina opita, mbadwo wina nufika; koma dziko lingokhalabe masiku onse,

5 inde dzuwa lituruka, nililowa, nilifulumira komwe linaturukako.

6 Kulowa kumwela ndi kuzungulira: kumpoto zungulire zungulire imaomba mphepo; ibweranso monga mwa mazunguliridwe ace.

7 Mitsinje yonse ithira m'nyanja, koma nyanja yosadzala; komwe imukira mitsinjeyo, komweko ibweranso.

8 Zinthu zonse zilemetsa; munthu sakhoza kuzifotokoza; maso sakhuta m'kuona, ndi makutu sakhuta m'kumva.

9 Comwe cinaoneka cidzaonekanso; ndi comwe cinacitidwa cidzacitidwanso; ndipo palibe kanthu katsopano pansi pano.

10 Kodi pali kanthu unganene kuti, Taona katsopano aka? Kanalipo kale, kale lomwe tisanabadwe ife.

11 Zoyamba zija sizikumbukiridwa; ngakhale zomwe zirinkudzazo, omwe adzakhalabe m'tsogolomo, sadzazikumbukirai.

12 Ine Mlaliki ndinali mfumu ya: Israyeli m'Yerusalemu.

13 Ndipo ndinapereka mtima kufunafuna ndi nzeru, ndi kulondetsa zonse zimacitidwa pansi pa thambo; nchito yobvuta imeneyi Mulungu apatsa ana a anthu akasauke nayo.

14 Ndaona nchito zonse zipangidwa kunja kuno; ndipo zonsezo ndi cabe ndi kungosautsa mtima.

15 Cokhotakhota sicingaongokenso; ndipo coperewera sicingawerengedwe.

16 Ndinalankhula ndi mtima wanga, ndi kuti, Taona, ndakuza ndi kudzienjezera nzeru koposa onse anakhala m'Yerusalemu ndisanabadwe ine; inde mtima wanga wapenyera kwambiri nzeru ndi cidziwitso.

17 Ndipo ndinapereka mtima kudziwa nzeru ndi kudziwa misala ndi utsiru; ndinazindikira kuti icinso cingosautsa mtima.

18 Pakuti m'nzeru yambiri muli cisoni cambiri; ndi yemwe aenjezera cidziwitso aenjezera zowawa.

Mitu

1 2 3 4 5 6 7 8 9 10 11 12