7 Ndaona akapolo atakwera pa akavalo, ndi mafumu, alikuyenda pansi ngati akapolo.
8 Wokumba mbuna adzagwamo; ndipo woboola mpanda njoka idzamluma.
9 Wosendeza miyala adzaphwetekedwa nayo; wowaza nkhuni nadzitema.
10 Citsulo cikakhala cosathwa, ndipo ukaleka kunola, uzipambana kulimbikira; koma nzeru ipindulira pocenjeza.
11 Njoka ikaluma isanalodzedwe, watsenga saona mphotho.
12 Mau a m'kamwa mwa munthu wanzeru nga cisomo; koma milomo ya citsiru idzacimeza.
13 Ciyambi ca mau a m'kamwa mwace ndi utsiru; ndipo cimariziro ca m'kamwa mwace ndi misala yoipa,