5 Citsiru cimanga manja ace, nicidya nyama yace yace.
6 Dzanja limodzi lodzala pali mtendere liposa manja awiri oti tho pali bvuto ndi kungosautsa mtima.
7 Pamenepo ndinabwera ndi kupenyera zacabe kunja kuno.
8 Pali mmodzi palibe waciwiri; inde, alibe mwana ngakhale mbale; koma nchito yace yonse iribe citsiriziro, ngakhale diso lace silikhuta cuma. Samati, Ndigwira nchito ndi kumana moyo wanga zabwino cifukwa ca yani? Icinso ndi cabe, inde, bvuto lalikuru.
9 Awiri aposa mmodzi; pakuti ali ndi mphotho yabwino m'nchito zao.
10 Pakuti akagwa, wina adzautsa mnzace; koma tsoka wakugwa wopanda womnyamutsa.
11 Ndiponso awiri akagona limodzi afunditsana; koma mmodzi pa yekha kodi adzafunditsidwa bwanji?