8 Pali mmodzi palibe waciwiri; inde, alibe mwana ngakhale mbale; koma nchito yace yonse iribe citsiriziro, ngakhale diso lace silikhuta cuma. Samati, Ndigwira nchito ndi kumana moyo wanga zabwino cifukwa ca yani? Icinso ndi cabe, inde, bvuto lalikuru.
9 Awiri aposa mmodzi; pakuti ali ndi mphotho yabwino m'nchito zao.
10 Pakuti akagwa, wina adzautsa mnzace; koma tsoka wakugwa wopanda womnyamutsa.
11 Ndiponso awiri akagona limodzi afunditsana; koma mmodzi pa yekha kodi adzafunditsidwa bwanji?
12 Ndipo wina akamlaka mmodziyo, awiri adzacirimika; ndipo cingwe ca nkhosi zitatu siciduka msanga.
13 Mnyamata wosauka ndi wanzeru apambana mfumu yokalamba ndi yopusa, imene sifunanso kulangidwa mwambo.
14 Pakuti aturuka m'nyumba yandende kulowa ufumu; komanso yemwe abadwa m'dziko lace asauka.