17 Usapambanitse kuipa, ngakhale kupusa, uferenji nthawi yako isanafike?
18 Kuli kwabwino kugwira ici; indetu, usacotsepo dzanja lako pakuti yemwe aopa Mulungu adzaturuka monsemo.
19 Nzeru ilimbitsa wanzeru koposa akuru khumi akulamulira m'mudzi.
20 Pakuti kulibe wolungama pansi pano amene acita zabwino osacimwa.
21 Mau onsetu onenedwa usawalabadire; kuti usamve kapolo wako alikukutemberera;
22 pakuti kawiri kawiritu mtima wako udziwa kuti nawenso unatemberera ena.
23 Ndayesa zonsezi ndi nzeru; ndinati, Ndidzakhala wanzeru, koma inanditarikira.