19 Nzeru ilimbitsa wanzeru koposa akuru khumi akulamulira m'mudzi.
20 Pakuti kulibe wolungama pansi pano amene acita zabwino osacimwa.
21 Mau onsetu onenedwa usawalabadire; kuti usamve kapolo wako alikukutemberera;
22 pakuti kawiri kawiritu mtima wako udziwa kuti nawenso unatemberera ena.
23 Ndayesa zonsezi ndi nzeru; ndinati, Ndidzakhala wanzeru, koma inanditarikira.
24 Cakutari ndi cakuyadi adzacipeza ndani?
25 Ndinapotoka ndi mtima wanga womwe kudziwa ndi kusanthula ndi kufunafuna nzeru ndi malongosoledwe a zinthu, ndi kudziwa kuti udio ndiwo utsiru, ndi kuti kupusa ndi misala;