25 Ndinapotoka ndi mtima wanga womwe kudziwa ndi kusanthula ndi kufunafuna nzeru ndi malongosoledwe a zinthu, ndi kudziwa kuti udio ndiwo utsiru, ndi kuti kupusa ndi misala;
26 ndipo ndinapeza kanthu kowawa koposa imfa, ndiko mkazi amene ndiye msampha, mtima wace ukunga maukonde, manja ace ndiwo matangadza; yemwe Mulungu amuyesa wabwino adzapulumuka kwa iye; koma wocimwa adzagwidwa naye.
27 Taonani, ici ndacipeza, ati Mlalikiyo, m'kuphatikiza cinthu cina ndi cinzace, ndikazindikire malongosoledwe ao;
28 comwe moyo wanga ucifuna cifunire, koma osacipezai ndi ici, mwamuna mmodzi mwa cikwi ndinampezadi, koma mkazitu mwa onsewo sindinampeza.
29 Taonani, ici cokha ndacipeza kuti Mulungu analenga anthu oongoka mtima; koma iwowo afunafuna malongosoledwe a mitundu mitundu.