15 koma anapezedwamo mwamuna wanzeru wosauka, yemweyo napulumutsa mudziwo ndi nzeru yace; koma panalibe anthu anakumbukira wosauka ameneyo.
16 Pamenepo ndinati, Nzeru ipambana mphamvu; koma anyoza nzeru ya wosauka, osamvera mau ace.
17 Mau a anzeru acete amveka koposa kupfuula kwa wolamulira mwa zitsiru.
18 Nzeru ipambana zida za nkhondo; koma wocimwa mmodzi aononga zabwino zambiri.