1 Cifukwa cace tiope kuti kapena likatsala lonjezano lakulowa mpumulo wace, wina wa inu angaoneke ngati adaliperewera.
2 Pakuti kwa ifenso walalikidwa Uthenga Wabwino, monganso kwa iwo; koma iwowa sanapindula nao mau omvekawo, popeza sanasanganizika ndi cikhulupiriro mwa iwo amene adawamva.
3 Popeza ife amene takhulupira tilowa mpumulowo, monga momwe ananena,Monga ndalumbira mu mkwiyowanga,Ngati adzalowa mpumulo wanga:zingakhale nebitozo zidatsirizika kuyambira kuzika kwa dziko lapansi.
4 Pakuti wanena pena za tsiku lacisanu ndi ciwiri, natero, Ndipo Mulungu anapumula tsiku lacisanu ndi ciwiri, kuleka nchito zace zonse
5 Ndipo m'menemonso,Ngati adzalowa mpumulo wanga.
6 Popeza tsono patsala kuti ena akalowa momwemo, ndi iwo amene Uthenga Wabwino unalalikidwa kwa iwo kale sanalowamo cifukwa ca kusamvera,