Ahebri 8 BL92

Cipangano cakale ndi cofanizira ndi copita, Kristu ali Nkhoswe ya cipangano cosatha

1 Koma mutu wafzi tanenazi ndi uwu: Tiri naye Mkuruwansembe wotere, amene anakhala pa dzanja lamanja la mpando wacifumu wa Ukulu m'Kumwamba,

2 Mtumiki wa malo opatulika, ndi wa cihema coona, cimene Ambuye anacimanga, si munthu ai.

3 Pakuti mkulu wa ansembe ali yense aikidwa kupereka mitulo, ndiponso nsembe; potero nkufunika kuti ameneyo akhale nako kanthunso kakupereka,

4 Ndipo iye akadakhala padziko, sakadakhala konse wansembe, popeza pali iwo akupereka mitulo monga mwa lamulo;

5 amene atumikira cifaniziro ndi mthunzi wa zakumwambazo monga Mose acenjezedwa m'mene anafuna kupanga cihema: pakuti, Cenjera, ati, ucite zonse monga mwa citsanzoco caonetsedwa kwa iwe m'phiri.

6 Koma tsopano iye walandira citumikiro comveka coposa, umonso ali Nkhoswe ya pangano labwino loposa, limene likhazikika pa malonjezano oposa.

7 Pakuti loyamba lija likadakhala lopanda cirema sakadafuna malo a laciwirilo.

8 Pakuti powachulira iwo cifukwa, anena,Taonani, akudza masiku, anena Ambuye,Ndipo ndidzapangana pangano latsopano ndi nyumba ya Israyeli, ndi nyumba ya Yuda,

9 Losati longa pangano ndinalicita ndi makolo ao,Tsikuli ndinawagwira kudzanja iwo kuwatsogolera aturuke m'dziko la Aigupto;Kuti iwo sanakhalabe m'pangano langa,Ndipo loe sindinawasamalira iwo, anena Ambuye,

10 Pakuti ili ndi pangano ndidzalipangana ndi nyumba ya Israyeli,Atapita masiku ajawa, anena Ambuye:Ndidzapatsa malamulo anga kuwalonga m'nzeru zao,Ndipo pamtima pao ndidzawalemba iwo;Ndipo ndidzawakhalira iwo Mulungu,Ndipo iwo adzandikhalira Ine anthu:

11 Ndipo sadzaphunzitsa yense mfulu mnzace,Ndipo yense mbale wace, ndi kuti, Zindikira Ambuye:Pakuti onse adzadziwa Ine, Kuyambira wamng'ono kufikira wamkuru wa iwo.

12 Kuti ndidzacitira cifundo rosalungama zao,Ndipo zoipa zao sindidzazikumbukanso.

13 Pakunena iye, Latsopano, anagugitsa loyambali. Koma cimene cirimkuguga ndi kusukuluka, cayandikira kukanganuka.

Mitu

1 2 3 4 5 6 7 8 9 10 11 12 13