10 Ndipo mbalewace wa munthu akamnyamula, ndiye womtentha, kuturutsa mafupa m'nyumba, nakati kwa iye ali m'kati mwa nyumbamo, Atsala wina nawe kodi? nakati, lai; pamenepo adzati, Khala cete; pakuti sitingachule dzina la Yehova.
11 Pakuti taonani, Yehova walamulira, nadzakantha nyumba yaikuru icite mpata, ndi nyumba yaing'ono icite mindala.
12 Kodi akavalo adzathamanga pathanthwe? kodi adzalimako ndi ng'ombe? pakuti mwasanduliza ciweruzo cikhale ndulu, ndi cipatso ca cilungamo cikhale civumulo;
13 inu okondwera naco copanda pace, ndi kuti, Kodi sitinadzilimbitsa tokha mwa mphamvu yathu yathu?
14 Pakuti taonani, ndidzakuutsirani mtundu wa anthu, nyumba ya Israyeli, ati Yehova Mulungu wa makamu; ndipo adzakupsinjani kuyambira polowera ku Hamati kufikira mtsinje wa kucidikha.