11 Mau a anzeru akunga zisonga, omwe akundika mau amene mbusa mmodzi awapatsa mau ao akunga misomali yokhomedwa zolimba.
12 Pamodzi ndi izi, mwananga, tacenjezedwa; pakuti saleka kulemba mabuku ambiri; ndipo kuphunzira kwambiri kutopetsa thupi.
13 Mau atha; zonse zamveka zatha; opa Mulungu, musunge malamulo ace; pakuti coyenera anthu onse ndi ici.
14 Pakuti Mulungu adzanena mlandu wa zocita zonse, ndi zobisika zonse, ngakhale zabwino ngakhale zoipa.