2 Ndipo ndinatama akufa atatha kufa kupambana amoyo omwe alipobe;
3 inde yemwe sanabadwe konse aposa onse awiriwo popeza sanaone nchito yoipa yocitidwa kunja kuno.
4 Ndiponso ndinapenyera mabvuto onse ndi nchito zonse zompindulira bwino, kuti cifukwa ca zimenezi anansi ace acitira munthu nsanje. Icinso ndi cabe ndi kungosautsa mtima.
5 Citsiru cimanga manja ace, nicidya nyama yace yace.
6 Dzanja limodzi lodzala pali mtendere liposa manja awiri oti tho pali bvuto ndi kungosautsa mtima.
7 Pamenepo ndinabwera ndi kupenyera zacabe kunja kuno.
8 Pali mmodzi palibe waciwiri; inde, alibe mwana ngakhale mbale; koma nchito yace yonse iribe citsiriziro, ngakhale diso lace silikhuta cuma. Samati, Ndigwira nchito ndi kumana moyo wanga zabwino cifukwa ca yani? Icinso ndi cabe, inde, bvuto lalikuru.