3 Cisoni ciposa kuseka; pakuti nkhope yakugwa ikonza mtima.
4 Mtima wa anzeru uli m'nyumba ya maliro; koma mtima wa zitsiru uli m'nyumba ya kuseka.
5 Kumva cidzudzulo ca anzeru kupambana kumva nyimbo ya zitsiru.
6 Pakuti kuseka kwa citsiru kunga minga irikutetheka pansi pa mphika; icinso ndi cabe.
7 Indetu nsautso iyarutsa wanzeru; ndi mtulo uipitsa mtima.
8 Citsiriziro ca kanthu ciposa ciyambi cace; wofatsa mtima apambana wodzikuza mtima.
9 Usakangaze mumtima mwako kukwiya; pakuti mkwiyo ugona m'cifuwa ca zitsiru.