14 Pamenepo ndinadula ndodo yanga yina, ndiyo Comanganitsa, kuti ndithetse cibale ca pakati pa Yuda ndi Israyeli.
15 Ndipo Yehova anati kwa ine, Dzitengerenso zipangizo za mbusa wopusa.
16 Pakuti taonani, ndidzautsa mbusa m'dziko amene sadzazonda otayika, kapena kufunafuna zomwazika, kapena kulunzitsa yotyoka, kapena kudyetsa yamoyo, koma adzadya nyama ya zonenepa, nadzang'amba ziboda zao.
17 Tsoka mbusa wopanda pace, wakusiya zoweta! lupanga pa dzanja lace, ndi pa diso lace la kumanja; dzanja lace lidzauma konse, ndi diso lace lamanja lidzada bii.