1 Ndipo kunacitika caka cacinai ca mfumu Dariyo, mau a Yehova anadza kwa Zekariya tsiku lacinai la mwezi wacisanu ndi cinai, ndiwo Kisilevi.
2 Ndipo a ku Beteli anatuma Sarezere ndi Regemeleke ndi anthu ao, apepeze Yehova,
3 nanene kwa ansembe a nyumba ya Yehova wa makamu, ndi kwa aneneri, ndi kuti, Kodi ndilire mwezi wacisanu, ndi kudzipatula, monga umo ndikacitira zaka izi zambiri?
4 Ndipo mau a Yehova wa makamu anadza kwa ine, ndi kuti,