22 Ndipo inu mwana wace, Belisazara inu, simunadzicepetsa m'mtima mwanu, cinkana munazidziwa izi zonse;
23 koma munadzikweza kutsutsana naye Ambuye wa Kumwamba; ndipo anabwera nazo zotengera za nyumba yace kwa inu; ndi inu ndi akuru anu, akazi anu ndi akazi anu ang'ono, mwamweramo vinyo; mwalemekezanso milungu yasiliva, ndi yagolidi, yamkuwa, yacitsulo, yamtengo, ndi yamwala, imene siiona, kapena kumva, kapena kudziwa; ndi Mulungu amene m'dzanja mwace muli mpweya wanu, ndi njira zanu zonse, yemweyo simunamcitira ulemu.
24 Pamenepo nsonga ya dzanja inatumidwa kucokera pamaso pace, nililembedwa lembali.
25 Ndipolembalolembedwa ndi ili: MENE MENE TEKEL UF ARSIN.
26 Kumasulira kwace kwa mau awa ndi uku: MENE, Mulungu anawerenga ufumu wanu, nautha.
27 TEKEL, Mwayesedwa pamiyeso, nimupezeka mwaperewera.
28 PERES, ufumu wanu wagawika, nuperekedwa kwa Amedi ndi Aperisi.