10 Pamenepo Estere ananena ndi Hataki, namtuma akauze Moredekai, ndi kuti,
11 Akapolo onse a mfumu ndi anthu a m'maiko a mfumu adziwa kuti ali yense, ngakhale wamwamuna kapena wamkazi, akalowa kwa mfumu ku bwalo la m'katimo wosaitanidwa, lamulo la pa iye ndi limodzi, ndilo kuti amuphe, akapanda mfumu kumloza ndi ndodo yacifumu yagolidi kuti akhale ndi moyo; koma ine sanaodiitana ndilowe kwa mfumu masiku awa makumi atatu.
12 Ndipo anamuuza Moredekai mau a Estere.
13 Koma Moredekai anawauza ambwezere mau Estere, kuti, Usamayesa m'mtima mwako kuti udzapulumuka m'nyumba ya mfumu koposa Ayuda onse ena.
14 Pakuti ukakhala cete konse tsopano lino, cithandizo ndi cipulumutso zidzafuma kwina; koma iwe ndi nyumba ya atate wako mudzaonongeka; ndipo kaya, kapena walowera ufumu cifukwa ca nyengo yonga iyi.
15 Pamenepo Estere anati ambwezere mau Moredekai,
16 Muka, sonkhanitsa Ayuda onse opezeka m'Susani, nimundisalire, osadya osamwa masiku atatu, usiku ndi usana, ine ndemwe ndi anamwali anga tidzasala momwemo, ndipo motero ndidzalowa kwa mfumu, ndiko kosalingana ndi lamulo; ndikaonongeka tsono ndionongeke,