Estere 8:9 BL92

9 Pamenepo anaitana alembi a mfumu nthawi yomweyo, mwezi wacitatu, ndiwo mwezi wa Sivani, tsiku lace la makumi awiri ndi citatu, monga mwa zonse Moredekai analamulira; nalembera kwa Ayuda ndi kwa akazembe, ndi ziwanga, ndi akalonga a kumaiko, oyambira ku Indiya, ofikira ku Kusi, maiko zana limodzi mphambu makumi awiri kudza asanu ndi awiri, ku dziko liri lonse monga mwa cilembedwe cao, ndi mtundu uli wonse monga mwa cinenedwe cao, ndi kwa Ayuda monga mwa cilembedwe cao, ndi monga mwa cinenedwe cao.

Werengani mutu wathunthu Estere 8

Onani Estere 8:9 nkhani